Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 8:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo ndidzalindira Yehova, amene wabisira a nyumba ya Yakobo nkhope yace, ndipo ndidzamyembekeza Iye,

18. Taonani, ine ndi ana amene Yehova wandipatsa ine, tiri zizindikilo ndi zodabwitsa mwa Israyeli, kucokera kwa Yehova wa makamu, amene akhala m'phiri la Ziyoni.

19. Ndipo pamene iwo adzati kwa iwe, Funa kwa olaula, ndi obwebweta, amene alira pyepye, nang'ung'udza; kodi anthu sadzafuna kwa Mulungu wao? Cifukwa ca amoyo, kodi adzafuna kwa akufa?

20. Kucilamulo ndi kuumboni! ngati iwo sanena malinga ndi mau awa, ndithu sadzaona mbanda kuca.

21. Ndipo iwo adzapitirira obvutidwa ndi anjala, ndipo padzakhala kuti pokhala ndi njala iwo adzadziputa okha, ndi kutemberera mfumu yao, ndi Mulungu wao; ndi kugadamira nkhope zao kumwamba;

22. nadzayang'ana padziko, koma taonani, nkhawa ndi mdima, kuziya kwa nsautso; ndi mdima woti bi udzaingitsidwa.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 8