Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 8:12-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Musacinene, Ciwembu; ciri conse cimene anthu awa adzacinena, Ciwembu; musaope monga kuopa kwao kapena musacite mantha.

13. Yehova wa makamu, Iye mudzamyeretsa; muope Iye, akucititseni mantha Iye.

14. Ndipo Iye adzakhala malo opatulika; koma mwala wopunthwitsa, ndi thanthwe lolakwitsa la nyumba zonse ziwiri za Israyeli, khwekhwe ndi msampha wa okhala m'Yerusalemu.

15. Ndipo ambiri adzapunthwapo, nagwa, natyoka, nakodwa, natengedwa.

16. Manga umboni, mata cizindikilo pacilamulo mwa aphunzi anga.

17. Ndipo ndidzalindira Yehova, amene wabisira a nyumba ya Yakobo nkhope yace, ndipo ndidzamyembekeza Iye,

18. Taonani, ine ndi ana amene Yehova wandipatsa ine, tiri zizindikilo ndi zodabwitsa mwa Israyeli, kucokera kwa Yehova wa makamu, amene akhala m'phiri la Ziyoni.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 8