Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 8:11-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Pakuti Yehova watero kwa ine ndi dzanja lolimba, nandilangiza ine kuti ndisayende m'njira ya anthu awa, nati,

12. Musacinene, Ciwembu; ciri conse cimene anthu awa adzacinena, Ciwembu; musaope monga kuopa kwao kapena musacite mantha.

13. Yehova wa makamu, Iye mudzamyeretsa; muope Iye, akucititseni mantha Iye.

14. Ndipo Iye adzakhala malo opatulika; koma mwala wopunthwitsa, ndi thanthwe lolakwitsa la nyumba zonse ziwiri za Israyeli, khwekhwe ndi msampha wa okhala m'Yerusalemu.

15. Ndipo ambiri adzapunthwapo, nagwa, natyoka, nakodwa, natengedwa.

16. Manga umboni, mata cizindikilo pacilamulo mwa aphunzi anga.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 8