Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 7:16-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Popeza kuti asanadziwe mwanayo kukana coipa ndi kusankha cabwino, dziko limene mafumu ace awiri udana nao lidzasyidwa.

17. Yehova adzatengera pa iwe, ndi pa anthu ako, ndi pa nyumba ya atate wako, masiku, akuti sanadze oterewa kuyambira tsiku limene Efraimu analekana ndi Yuda; kunena mfumu ya Asuri.

18. Ndipo padzakhala tsiku limenelo kuti Yehova adzayimbira mluzu cimphanga ciri m'mbali ya kumtunda kwa nyanja za Aigupto, ndi njuci iri m'dziko la Asuri.

19. Ndipo zidzafika nizitera zonse m'zigwa zabwinja, ndi m'maenje a matanthwe, ndi paminga ponse, ndi pamabusa ponse.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 7