Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 6:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo ine ndinati, Tsoka kwa ine! cifukwa ndathedwa; cifukwa ndiri munthu wa milomo yonyansa, ndikhala pakati pa anthu a milomo yonyansa; cifukwa kuti maso anga aona Mfumu, Yehova wa makamu.

6. Pompo anaulukira kwa ine mmodzi wa aserafi, ali nalo khala lamoto m'dzanja mwace, limene analicotsa ndi mbaniro pa guwa la nsembe;

7. nakhudza nalo kukamwa kwanga nati, Taona ici cakhudza milomo yako; ndipo mphulupulu zako zacotsedwa, zocimwa zako zaomboledwa.

8. Ndipo ndinamva mau a Ambuye akuti, Ndidzatumiza yani, ndipo ndani adzatimukira ife? Ndipo ine ndinati, Ndine pano; munditumize ine.

9. Ndipo Iye anati, Kauze anthu awa, Imvani inu ndithu, koma osazindikira; yang'anani inu ndithu, koma osadziwitsa.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 6