Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 57:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Wolungama atayika, ndipo palibe munthu wosamalirapo; ndipo anthu acifundo atengedwa, palibe wolingalira kuti wolungama acotsedwa pa coipa cirinkudza.

2. Iye alowa mumtendere, iwo apuma pa mphasa zao, yense woyenda moongoka.

3. Koma sendererani kuno cifupi, inu ana amuna a watsenga, mbeu yacigololo ndi yadama.

4. Ndiye yani mudzikondweretsa momseka? Ndani mulikumyasamira kukamwa, ndi kumturutsira lilime? Kodi inu simuli ana akulakwa, mbeu yonama?

Werengani mutu wathunthu Yesaya 57