Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 5:11-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Tsoka kwa iwo amene adzuka m'mamawa kuti atsate zakumwa zaukali; amene acezera usiku kufikira vinyo awaledzeretsal

12. Ndipo zeze ndi mgoli, ndi lingaka ndi citoliro, ndi vinyo, ziri m'mapwando ao; koma iwo sapenyetsa nchito ya Yehova; ngakhale kuyang'ana pa macitidwe a manja ace.

13. Cifukwa cace anthu anga amuka m'nsinga, cifukwa ca kusowa nzeru; ndi amuna ao olemekezeka ali ndi njala, ndi khamu lao lauma kukhosi.

14. Ndipo manda akuza cilakolako cace, natsegula kukamwa kwace kosayeseka; ndi ulemerero wao, ndi unyinji wao, ndi phokoso lao, ndi iye amene akondwerera mwa iwo atsikira mommo.

15. Munthu wonyozeka waweramitsidwa, ndi munthu wochuka watsitsidwa, ndi maso a wodzikweza atsitsidwa;

16. koma Yehova wa makamu wakwezedwa m'ciweruziro, ndipo Mulungu Woyera wayeretsedwa m'cilungamo.

17. Pamenepo ana a nkhosa adzadyapo ngati m'busa mwao, ndi malo a bwinja a zonenepa zacilendo zidzadyapo.

18. Tsoka kwa iwo amene akoka mphulupulu ndi zingwe zacabe, ndi cimo ngati ndi cingwe ca gareta;

19. amene ati, Mlekeni iye akangaze, mlekeni iye afulumize nchito yace kuti ife tione; ndipo lekani uphungu wa Woyera wa Israyeli uyandikire, udze kuti tiudziwe!

20. Tsoka kwa iwo amene ayesa zoipa zabwino, ndi zabwino zoipa; amene aika mdima m'malo mwa kuyera, ndi kuyera m'malo mwa mdima; amene aika zowawa m'malo mwa zotsekemera, ndi zotsekemera m'malo mwa zowawa!

Werengani mutu wathunthu Yesaya 5