Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 48:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Inde dzanja langa linakhazika maziko a dziko lapansi, ndi dzanja langa lamanja linafunyulula m'mwamba; pakuziitana Ine ziimirira pamodzi.

14. Sonkhanani inu nonse ndi kumva, ndani mwa iwo aonetsa zinthu izi? Iye amene Yehova anamkonda, iye adzacita kufuna kwace pa Babulo, ndi mkono wace udzakhala pa Akasidi.

15. Ine, ngakhale Ine ndanena; inde ndamwitana iye, ndamfikitsa, ndipo adzapindula nayo njira yace.

16. Idzani inu cifupi ndi Ine, imvani ici; kuyambira pa ciyambi sindinanene m'tseri; ciyambire zimenezi, Ine ndiripo; ndipo tsopano Ambuye Mulungu wanditumiza Ine ndi mzimu wace.

17. Atero Yehova, Mombolo wako, Woyera wa Israyeli, Ine ndine Yehova, Mulungu wako, amene ndikuphunzitsa kupindula, amene ndikutsogolera m'njira yoyenera iwe kupitamo.

18. Mwenzi utamvera malamulo anga mtendere wako ukanakhala ngati mtsinje, ndi cilungamo cako monga mafunde a nyanja;

Werengani mutu wathunthu Yesaya 48