Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 46:7-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Iwo amanyamula mlunguwu paphewa, nausenza, naukhazika m'malo mwace, nukhala ciriri; pamalo pacepo sudzasunthika; inde, wina adzaupfuulira, koma sungathe kuyankha, kapena kumpulumutsa m'zobvuta zace.

8. Kumbukirani ici, nimucirimike, mudzikumbutsenso, olakwa inu.

9. Kumbukirani zinthu zoyamba zakale, kuti Ine ndine Mulungu, ndipo palibenso wina; Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina wofana ndi Ine;

Werengani mutu wathunthu Yesaya 46