Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 43:25-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Ine, Inedi, ndine amene ndifafaniza zolakwa zako, cifukwa ca Ine mwini; ndipo Ine sindidzakumbukira macimo ako.

26. Undikumbutse Ine; tiyeni, tinenane pamodzi; fotokoza mlandu wako, kuti ukalungamitsidwe.

27. Atate wako woyamba anacimwa, ndi otanthauzira ako andilakwira Ine.

28. Cifukwa cace ndidzaipitsa akuru a kacisi, ndipo ndidzasanduliza Yakobo akhale temberero, ndi Israyeli akhale citonzo.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 43