Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 43:2-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Pamene udulitsa pamadzi ndiri pamodzi ndi iwe; ndi pooloka mitsinje sidzakukokolola; pakupyola pamoto sudzapsya; ngakhale lawi silidzakutentha.

3. Cifukwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wako, Woyera wa Israyeli, Mpulumutsi wako; ndapatsa Aigupto dombolo lako, Etiopia ndi Seba m'malo mwako.

4. Pokhala iwe wa mtengo wapatari pamaso panga, ndi wolemekezeka, ndipo ndakukonda iwe; Ine ndidzakuombola ndi anthu, ndi kupereka anthu m'malo mwa moyo wako.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 43