Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 43:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Inde ciyambire nthawi Ine ndine, ndipo palibe wina wopulumutsa m'dzanja langa; ndidzagwira nchito, ndipo ndani adzaletsa?

14. Atero Yehova, Mombolo wanu, Woyera wa Israyeli: Cifukwa ca inu ndatumiza ku Babulo, ndipo ndidzatsitsira iwo onse monga othawa, ngakhale Akasidi m'ngalawa za kukondwa kwao.

15. Ine ndine Yehova Woyera wanu, Mlengi wa Israyeli, Mfumu yanu,

16. Atero Yehova, amene akonza njira panyanja, ndi popita m'madzi amphamvu;

Werengani mutu wathunthu Yesaya 43