Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 40:12-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndani wayesa madzi m'dzanja lace, nayesa thambo ndi cikhato, ndi kudzaza pfumbi la nthaka m'nsengwa, ndi kuyesa mapiri m'mbale zoyesera, ndi zitunda m'mulingo?

13. Ndani anapangira mzimu wa Yehova, kapena kukhala phungu lace, ndi kumphunzitsa Iye?

14. Iye anakhala upo ndi yani, ndipo ndani analangiza Iye ndi kumphunzitsa m'njira ya ciweruzo, ndi kumphunzitsa nzeru ndi kumuonetsa njira ya luntha?

15. Taonani, amitundu akunga dontho la m'mtsuko, nawerengedwa ngati pfumbi losalala la m'muyeso; taonani atukula zisumbu ngati kanthu kakang'ono.

16. Ndipo Lebano sakwanira kutentha, ngakhale nyama zace sizikwanira nsembe yopsereza.

17. Amitundu onse ali cabe pamaso pa Iye; awayesa ngati cinthu cacabe, ndi copanda pace,

18. Mudzafanizira Mulungu ndi yani tsopano, kapena kumyerekeza ndi cithunzithunzi cotani?

19. Pano losema mmisiri analisungunula, ndipo wosula golidi analikuta ndi golidi, naliyengera maunyolo asiliva.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 40