Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 39:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo iye anati, Kodi iwo anaona ciani m'nyumba mwanu? Ndipo Hezekiya anayankha, Zonse za m'nyumba mwanga iwo anaziona; palibe kanthu ka mwa cuma canga, kamene ine sindinawaonetse.

5. Ndipo Yesaya anati kwa Hezekiya, Imvani mau a Yehova wa makamu.

6. Taona, masiku afika, kuti zonse za m'nyumba mwako, ndi zimene atate ako anazikundika kufikira lero lino, zidzatengedwa kunka ku Babulo; sipadzatsala kanthu, ati Yehova.

7. Ndipo ana ako amene adzabadwa ndi iwe, amene udzabala, iwo adzawatenga, ndipo adzakhala adindo m'cinyumba cace ca mfumu ya ku Babulo.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 39