1. Tsoka kwa iwe amene usakaza, cinkana sunasakazidwa; nupangira ciwembu, cinkana sanakupangira iwe ciwembu! Utatha kusakaza, iwe udzasakazidwa; ndipo utatha kupangira ciwembu, iwo adzakupangira iwe ciwembu.
2. Inu Yehova, mutikomere ife mtima; ife talindira Inu; mukhale dzanja lathu m'mawa ndi m'mawa, cipulumutso cathunso m'nthawi ya mabvuto.
3. Pa mau a phokoso mitundu ya anthu yathawa; ponyamuka iwe amitundu abalalika,
4. Ndipo zofunkha zanu zidzasonkhanitsidwa, monga ziwala zisonkhana; monga madzombe atumpha, iwo adzatumpha pa izo.
5. Yehova wakwezedwa; pakuti akhala kumwamba; Iye wadzaza Ziyoni ndi ciweruzo ndi cilungamo.
6. Ndipo kudzakhala cilimbiko m'nthawi zako, cipulumutso cambiri, nzeru ndi kudziwa; kuopa kwa Yehova ndiko cumacace.
7. Taonani, olimba mtima ao angopfuula kunja, mithenga ya mtendere ilira kowawa.
8. Njira zamakwalala zikufa, kulibe woyendamo; Asuri watyola cipangano, wanyoza midzi, sasamalira anthu.
9. Dziko lilira maliro ndi kulefuka; Lebano ali ndi manyazi, nafota; Saroni afanana ndi cipululu; pa Basana ndi Karimeli papukutika.
10. Tsopano ndidzauka, ati Yehova; tsopano ndidzanyamuka, tsopano ndidzakwezedwa.
11. Inu mudzatenga pakati ndi mungu, mudzabala ziputu; mpweya wanu ndi moto umene udzakumarizani inu.