Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 32:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Taonani mfumu idzalamulira m'cilungamo, ndi akalonga adzalamulira m'ciweruzo.

2. Ndipo munthu adzakhala monga pobisalira mphepo, ndi pousira cimphepo; monga mitsinje yamadzi m'malo ouma, monga mthunzi wa thanthwe lalikuru m'dziko lotopetsa.

3. Ndipo maso a iwo amene aona sadzatsinzina, ndi makutu a iwo amene amva adzamvera.

4. Mtimanso wansontho udzadziwa nzeru, ndi lilume la acibwibwi lidzalankhula zomveka msanga.

5. Wopusa sadzayesedwanso woolowa manja, ngakhale wouma manja sadzayesedwa mfulu.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 32