Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 32:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Taonani mfumu idzalamulira m'cilungamo, ndi akalonga adzalamulira m'ciweruzo.

2. Ndipo munthu adzakhala monga pobisalira mphepo, ndi pousira cimphepo; monga mitsinje yamadzi m'malo ouma, monga mthunzi wa thanthwe lalikuru m'dziko lotopetsa.

3. Ndipo maso a iwo amene aona sadzatsinzina, ndi makutu a iwo amene amva adzamvera.

4. Mtimanso wansontho udzadziwa nzeru, ndi lilume la acibwibwi lidzalankhula zomveka msanga.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 32