Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 32:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Taonani mfumu idzalamulira m'cilungamo, ndi akalonga adzalamulira m'ciweruzo.

2. Ndipo munthu adzakhala monga pobisalira mphepo, ndi pousira cimphepo; monga mitsinje yamadzi m'malo ouma, monga mthunzi wa thanthwe lalikuru m'dziko lotopetsa.

3. Ndipo maso a iwo amene aona sadzatsinzina, ndi makutu a iwo amene amva adzamvera.

4. Mtimanso wansontho udzadziwa nzeru, ndi lilume la acibwibwi lidzalankhula zomveka msanga.

5. Wopusa sadzayesedwanso woolowa manja, ngakhale wouma manja sadzayesedwa mfulu.

6. Pakuti wopusa adzanena zopusa, ndi mtima wace udzacita mphulupulu, kucita zoipitsa, ndi kunena za Yehova molakwira, kusowetsa konse mtima wanjala, ndi kulepheretsa cakumwa ca waludzu.

7. Zipangizonso za womana ziri zoipa; iye apangira ziwembu zakuononga waumphawi ndi mau onama, ngakhale pamene wosowa alankhula zoona.

8. Koma mfulu aganizira zaufulu, nakhazikika m'zaufulu zomwe.

9. Ukani, akazi inu, amene mulinkukhala phe, mumve mau anga; mu ana akazi osasamalira, cherani makutu pa kulankhula kwanga.

10. Pakutha caka, kudza masiku ena inu mudzabvutidwa, inu akazi osasamalira; pakuti masika a mphesa adzasoweka, sadzatuta konse.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 32