Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 3:2-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. munthu wamphamvu, ndi munthu wankhondo; woweruza, ndi mneneri, ndi waula, ndi nkhalamba;

3. kapitao wa makumi asanu, ndi munthu wolemekezeka, ndi mphungu, ndi mmisiri waluso, ndi wodziwa matsenga.

4. Ndipo ndidzapereka ana, kuti akhale akuru ao, mwacibwana adzawalamulira.

5. Ndi anthu adzabvutidwa, yense ndi wina, yense ndi mnansi wace; mwana adzadzinyaditsa yekha pa akuru, ndi onyozeka pa olemekezedwa.

6. Pamene mwamuna adzamgwira mbale wace m'nyumba ya atate wace, nadzati, Iwe uli ndi cobvala, khala wolamulira wathu, ndi kupasula kumeneku kukhale m'dzanja lako;

7. tsiku limenelo adzakweza mau ace, kuti, Sindine wociritsa, cifukwa kuti m'nyumba mwanga mulibe cakudya kapena cobvala; inu simudzandiyesa ine wolamulira anthu.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 3