Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 23:7-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Kodi umene ndi mudzi wanu wokondwa, wacikhalire kale lomwe, umene mapazi ace anaunyamula kunka nao kutari kukhalako?

8. Ndani wapanga uphungu uno pa Turo, mudzi umene upereka akorona, amalonda ace ali akalonga, ogulitsa ace ali olemekezeka pa dziko lapansi?

9. Yehova wa makamu wapanga uphungu uwu, kuipitsa kunyada kwa ulemerero wonse, kupepula onse olemekezeka a m'dziko lapansi.

10. Pita pakati pa dziko lako monga Nile, iwe mwana wamkazi wa Tarisi; palibenso lamba.

11. Iye watambasula dzanja lace panyanja, wagwedeza maufumu; Yehova walamulira za amalonda, kupasula malinga ace.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 23