Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 22:1-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Katundu wa cigwa ca masomphenya.Mwatani kuti mwakwera nonsenu pamacindwi?

2. Iwe amene wadzala ndi zimpfuu, mudzi waphokoso, mudzi wokondwa; ophedwa ako, sanaphedwa ndi lupanga, sanafe m'nkhondo.

3. Olamulira ako onse athawa pamodzi, anamangidwa ndi amauta; opezedwa ako onse anamangidwa pamodzi, nathawira patari.

4. Comweco ndinati, Usandiyang'ane ine, ndilira ndi kuwawa mtima; usafulumire kunditonthoza ine, cifukwa ca kufunkhidwa kwa mwana wamkazi wa anthu anga,

5. Pakuti ndi tsiku laphokoso, ndi lopondereza pansi, ndi lothetsa nzeru, locokera kwa Ambuye Yehova wa makamu, m'cigwa ca masomphenya, kugumuka kwa malinga, ndi kupfuulira kumapiri.

6. Ndipo Elamu anatenga phodo, ndi magareta a anthu ndi apakavalo; ndipo Kiri anaonetsa zikopa.

7. Ndipo panali kuti zigwa zako zosankhika zinadzala magareta, ndi apakavalo anadzinika okha pacipata.

8. Ndipo Iye anacotsa cophimba ca Yuda; ndipo iwe unayang'ana tsiku limenelo pa zida za m'nyumba ya nkhalango.

9. Ndipo inu munaona kuti pa mudzi wa Davide panagumuka mipata yambiri; ndipo munasonkhanitsa pamodzi madzi a m'thamanda lakunsi.

10. Ndipo inu munawerenga nyumba za Yerusalemu, ndipo munagwetsa nyumba, kuti mumangire linga.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 22