Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 21:12-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Mlonda anati, Kuli kuca, koma kukali usiku; mukafuna kufunsa, funsani, bwerani, idzani.

13. Katundu wa pa Arabiya.M'nkhalango ya m'Arabiya mudzagona, inu makamu oyendayenda a Dedani.

14. Mucingamire akumva ludzu ndi madzi; okhala m'dziko la Tema ananka kukomana ndi othawa ndi cakudya cao.

15. Pakuti iwo anathawa malupanga, malupanga osololedwa, ndi mauta-olifuka ndi nkhondo yobvuta.

16. Pakuti Ambuye ana tero kwa ine, Cisanapite caka malinga ndi zaka za wolembedwa nchito ulemerero wonse wa Kedara udzagoma;

17. ndi otsala amauta, ngwazi za ana a Kedara zidzacepa, pakuti Yehova Mulungu wa Israyeli wanena.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 21