11. Katundu wa Duma.Wina aitana kwa ine kucokera ku Seiri, Mlonda, nthawi yanji ya usiku? Mlonda, nthawi yanji ya usiku?
12. Mlonda anati, Kuli kuca, koma kukali usiku; mukafuna kufunsa, funsani, bwerani, idzani.
13. Katundu wa pa Arabiya.M'nkhalango ya m'Arabiya mudzagona, inu makamu oyendayenda a Dedani.
14. Mucingamire akumva ludzu ndi madzi; okhala m'dziko la Tema ananka kukomana ndi othawa ndi cakudya cao.
15. Pakuti iwo anathawa malupanga, malupanga osololedwa, ndi mauta-olifuka ndi nkhondo yobvuta.
16. Pakuti Ambuye ana tero kwa ine, Cisanapite caka malinga ndi zaka za wolembedwa nchito ulemerero wonse wa Kedara udzagoma;