Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 21:11-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Katundu wa Duma.Wina aitana kwa ine kucokera ku Seiri, Mlonda, nthawi yanji ya usiku? Mlonda, nthawi yanji ya usiku?

12. Mlonda anati, Kuli kuca, koma kukali usiku; mukafuna kufunsa, funsani, bwerani, idzani.

13. Katundu wa pa Arabiya.M'nkhalango ya m'Arabiya mudzagona, inu makamu oyendayenda a Dedani.

14. Mucingamire akumva ludzu ndi madzi; okhala m'dziko la Tema ananka kukomana ndi othawa ndi cakudya cao.

15. Pakuti iwo anathawa malupanga, malupanga osololedwa, ndi mauta-olifuka ndi nkhondo yobvuta.

16. Pakuti Ambuye ana tero kwa ine, Cisanapite caka malinga ndi zaka za wolembedwa nchito ulemerero wonse wa Kedara udzagoma;

Werengani mutu wathunthu Yesaya 21