Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 2:6-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Cifukwa inu mwasiya anthu anu a nyumba ya Yakobo, cifukwa kuti iwo adzazidwa ndi miyambo ya kum'mawa, ndipo ali olaula ngati Afilisti, naomba m'manja ndi ana a acilendo.

7. Dziko lao ladzala siliva ndi golidi, ngakhale cuma cao ncosawerengeka; dziko lao lidzalanso akavalo, ngakhale magareta ao ngosawerengeka.

8. Dziko lao ladzalanso mafano; iwo apembedza nchito ya manja ao ao, imene zala zao zao zinaipanga.

9. Munthu wacabe agwada pansi, ndi munthu wamkuru adzicepetsa, koma musawakhululukire.

10. Lowa m'phanga, bisala m'pfumbi, kucokera pa kuopsya kwa Yehova, ndi pa ulemerero wacifumu wace.

11. Maso a munthu akuyang'anira kumwamba adzatsitsidwa, ndi kudzikweza kwa anthu kudzaweramitsidwa pansi; ndipo Yehova yekha adzakwezedwa tsiku limenelo.

12. Cifukwa padzakhala tsiku la Yehova wa makamu pa zonse zonyada ndi zakudzikuza, ndi pa zonse zotukulidwa; ndipo zidzatsitsidwa;

Werengani mutu wathunthu Yesaya 2