Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 19:3-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo mzimu wa Aigupto adzakhala wacabe pakati pace; ndipo Ine ndidzaononga uphungu wace; ndimo iwo adzafunafuna mafano ndi anyanga, ndi alauli, ndi obwebweta.

4. Ndipo ndidzapereka Aigupto m'manja mwa mbuye wankharwe; ndi mfumu yaukali idzawalamulira, ati Ambuye, Yehova wa makamu.

5. Ndipo madzi adzaphwa m'nyanja yaikuru, ndipo nyanja yoyendamo madzi idzaphwa, niuma.

6. Ndipo nyanja zidzanunkha; mitsinje ya Aigupto idzacepa, niuma; bango ndi mlulu zidzafota.

7. Madambo ovandikana ndi Nile, pafupi ndi gombe la Nile, ndi zonse zobzyala pa Nile zidzauma, nizicotsedwa, zosakhalanso konse.

8. Asodzinso adzalira, ndi onse oponya mbedza m'Nile adzaliralira, ndi onse oponya makoka m'madzi, adzalefuka.

9. Komanso iwo amene agwira nchito yakupala bwazi, ndi iwo amene aomba nsaru yoyera, adzakhala ndi manyazi.

10. Ndipo maziko ace adzasweka, onse amene agwira nchito yolipidwa adzabvutidwa mtima.

11. Akalonga a Zoani apusa ndithu; uphungu wa aphungu anzeru a Farao wasanduka wopulukira; bwanji iwe unena kwa Farao, Ine ndine mwana wa anzeru, mwana wa mafumu akale?

12. Nanga tsopano anzeru ali kuti? akuuze iwe tsopano; adziwe cimene Yehova wa makamu watsimikiza mtima kucitira Aigupto.

13. Akalonga a Zoani apusa, akalonga a Nofi anyengedwa; iwo asoceretsa Aigupto, amene ali mwala wa pangondya wa mapfuko ace.

14. Yehova wasanganiza mzimu wa kusaweruzika pakati pace; ndipo iwo asoceretsa Aigupto m'nchito zonse zace, monga mwamuna woledzera ayenda punzipunzi posanza pace.

15. Aigupto sadzakhala ndi nchito, imene mutu pena mcira, pena nthambi ya kanjedza, pena mlulu zidzaigwira.

16. Tsiku limenelo Aigupto adzanga akazi; ndipo adzanthunthumira ndi kuopa, cifukwa ca kugwedeza kwa dzanja la Yehova wa makamu, limene Iye agwedeza pamwamba pace.

17. Ndipo dziko la Yuda lidzaopsa Aigupto, yense wakulichula adzamtembenukira mwamantha, cifukwa ca uphungu wa Yehova wa makamu, aupanga pa dzikolo.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 19