Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 19:14-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Yehova wasanganiza mzimu wa kusaweruzika pakati pace; ndipo iwo asoceretsa Aigupto m'nchito zonse zace, monga mwamuna woledzera ayenda punzipunzi posanza pace.

15. Aigupto sadzakhala ndi nchito, imene mutu pena mcira, pena nthambi ya kanjedza, pena mlulu zidzaigwira.

16. Tsiku limenelo Aigupto adzanga akazi; ndipo adzanthunthumira ndi kuopa, cifukwa ca kugwedeza kwa dzanja la Yehova wa makamu, limene Iye agwedeza pamwamba pace.

17. Ndipo dziko la Yuda lidzaopsa Aigupto, yense wakulichula adzamtembenukira mwamantha, cifukwa ca uphungu wa Yehova wa makamu, aupanga pa dzikolo.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 19