Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 10:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Iwe Asuri cibonga ca mkwiyo wanga, ndodo m'dzanja lace muli ukali wanga!

6. Ine ndidzamtumiza kumenyana ndi mtundu wosalemekeza, ndi pa anthu a mkwiyo wanga ndidzamlangiza, kuti afunkhe, agwire zolanda, awapondereze pansi, monga dothi la pamakwalala.

7. Koma iye safuna cotero, ndipo mtima wace suganizira cotero, koma mtima wace ulikufuna kusakaza, ndi kuduladula amitundu osawerengeka.

8. Popeza ati, Akalonga anga kodi sali onse mafumu?

9. Kodi Kalino sali wonga ngati Karikemesi? kodi Hamati sali ngati Aripadi? kodi Samariya sali ngati Damasiko?

Werengani mutu wathunthu Yesaya 10