Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 10:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Tsoka kwa iwo amene alamulira malamulo osalungama, ndi kwa alembi olemba mphulupulu;

2. kuwapatulira osowa kuciweruziro, ndi kucotsera anthu anga aumphawi zoyenera zao, kuti alande za akazi amasiye, nafunkhire ana amasiye!

3. Ndipo mudzacita ciani tsiku lakudza woyang'anira, ndi cipasuko cocokera kutari? mudzathawira kwa yani kufuna kuthangatidwa? mudzasiya kuti ulemerero wanu?

4. Adzangoweramira pansi pa andende, ndipo adzagwa pansi pa ophedwa. Mwa izi zonse mkwiyo wace sunacoke, koma dzanja lace liri citambasulire.

5. Iwe Asuri cibonga ca mkwiyo wanga, ndodo m'dzanja lace muli ukali wanga!

Werengani mutu wathunthu Yesaya 10