Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yesaya 1:27-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Ziyoni adzaomboledwa ndi ciweruzo, ndi otembenuka mtima ace ndi cilungamo.

28. Koma kupasula kwa olakwa ndi kwa ocimwa kudzakhala kumodzi, ndi iwo amene asiya Yehova adzathedwa.

29. Cifukwa adzakhala ndi manyazi, cifukwa ca mitengo yathundu munaikhumba, ndipo inu mudzagwa nkhope, cifukwa ca minda imene mwaisankha.

30. Cifukwa mudzakhala ngati mtengo wathundu, umene tsamba lace linyala, ngatinso munda wopanda madzi.

31. Ndimo wamphamvu adzakhala ngati cingwe cabwazi, ndi nchito yace ngati nthethe; ndipo zonse zidzayaka moto pamodzi, opanda wozimitsa.

Werengani mutu wathunthu Yesaya 1