Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 7:5-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Pakuti mukakonzatu njira zanu ndi macitidwe anu; ndi kuweruzatu milandu ya munthu ndi mnansi wace;

6. ndi kuleka kutsendereza mlendo, ndi wamasiye, ndi mkazi wamasiye, osakhetsa mwazi wosacimwa m'malo muno, osatsata milungu yina ndi kudziipitsa nayo;

7. ndipo ndidzakukhazikani inu m'malo muno, m'dziko limene ndinapatsa makolo anu, kuyambira kale lomwe kufikira muyaya,

8. Taonani, mukhulupirira mau onama, osapindulitsa.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 7