Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 7:2-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ima m'cipata ca nyumba ya Yehova, lalikira m'menemo mau awa, ndi kuti, Tamvani mau a Yehova, inu nonse a Yuda, amene alowa m'zipata izi kuti mugwadire Yehova.

3. Yehova wa makamu atero, Mulungu wa Israyeli, Konzani njira zanu ndi macitidwe anu, ndipo ndidzakukhalitsani inu m'malo ano.

4. Musakhulupirire mau onama, kuti, Kacisi wa Yehova, kacisi wa Yehova, kacisi wa Yehova ndi awa.

5. Pakuti mukakonzatu njira zanu ndi macitidwe anu; ndi kuweruzatu milandu ya munthu ndi mnansi wace;

6. ndi kuleka kutsendereza mlendo, ndi wamasiye, ndi mkazi wamasiye, osakhetsa mwazi wosacimwa m'malo muno, osatsata milungu yina ndi kudziipitsa nayo;

7. ndipo ndidzakukhazikani inu m'malo muno, m'dziko limene ndinapatsa makolo anu, kuyambira kale lomwe kufikira muyaya,

8. Taonani, mukhulupirira mau onama, osapindulitsa.

9. Kodi mudzapha, ndi kuba, ndi kucita cigololo, ndi kulumbira zonama, ndi kupereka nsembe kwa Baala, ndi kutsata milungu yina imene simunaidziwa,

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 7