Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 7:14-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. cifukwa cace ndidzaicitira nyumba iyi, imene ichedwa dzina langa, imene mukhulupirirayi, ndipo ndidzacitira malo amene ndinakupatsani inu ndi makolo anu, monga ndinacitira Silo.

15. Ndipo ndidzakucotsani inu pamaso panga, monga ndinacotsa abale anu onse, mbeu zonse za Efraimu.

16. Cifukwa cace iwe usapempherere anthu awa, usawakwezere iwo mpfuu kapena pemphero, usandipembedze; pakuti Ine sindidzakumvera iwe.

17. Kodi suona iwe cimene acicita m'midzi ya Yuda ndi m'miseu ya Yerusalemu?

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 7