Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 6:27-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Ndakuyesa iwe nsanja ndi linga mwa anthu anga, kuti udziwe ndi kuyesa njira yao.

28. Onse ali opikisana ndithu, ayendayenda ndi maugogodi; ndiwo mkuwa ndi citsulo; onsewa acita mobvunda;

29. mbvukuto yatenthedwa ndi moto; mthobvu watha ndi moto wa ng'anjo; ayenga cabe; pakuti oipa sacotsedwa.

30. Anthu adzawacha nthale ya siliva, pakuti Yehova wakana iwo.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 6