Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 51:60-64 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

60. Ndipo Yeremiya analemba m'buku coipa conse cimene cidzafika pa Babulo, mau onse awa olembedwa za Babulo.

61. Ndipo Yeremiya anati kwa Seraya, Pamene ufika ku Babulo, samalira kuti uwerenge mau awa onse,

62. nuti, inu Yehova, mwanena za malo ano, kuti mudzawatha, kuti asakhalemo, ngakhale anthu ngakhale nyama, koma akhale bwinja nthawi za nthawi.

63. Ndipo padzakhala, utatha kuwerenga buku ili, Ib ulimange ndi mwala, nuliponye pakati pa Firate;

64. nuti, Comweco adzamira Babulo, sadzaukanso cifukwa ca coipa cimene ndidzamtengera iye; ndipo adzatopa.Mau a Yeremiya ndi omwewo.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 51