Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 51:38-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

38. Adzabangula pamodzi ngati misona ya mikango; adzacita nthulu ngati ana a mikango.

39. Pamene atentha, ndidzakonza madyerero ao, ndidzawaledzeretsa, kuti asangalale, agone cigonere, asanyamuke, ati Yehova.

40. Ndidzawagwetsa kuti aphedwe manga nkhosa zamphongo, ndi atonde.

41. Sesake wagwidwatul cimene dziko lonse lapansi linacitamanda calandidwa dzidzidzi Babulo wakhalatu bwinja pakati pa amitundu

42. Nyanja yakwera kufikira ku Babulo; wamira ndi mafunde ace aunyinji.

43. Midzi yace yakhala bwinja, dziko louma, cipululu mosakhalamo anthu, mosapita mwana wa munthu ali yense.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 51