Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 5:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Thamangani inu kwina ndi kwina m'miseu ya Yerusalemu, taonanitu, dziwani, ndi kufunafuna m'mabwalo ace, kapena mukapeza munthu, kapena alipo wakucita zolungama, wakufuna coonadi; ndipo ndidzamkhululukira.

2. Ndipo ngakhale ati, Pali Yehova; komatu alumbira monama.

3. Yehova Inu, maso anu sali pacoonadi kodi? munawapanda iwo, koma sanaphwetekedwa mtima; munawatha iwo, koma akana kudzudzulidwa; alimbitsa nkhope zao koposa mwala; akana kubwera.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 5