Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 48:36-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

36. Cifukwa cace mtima wanga umlima Moabu monga zitolilo, ndipo mtima wanga uwalirira anthu a Kireresi monga zitolilo, cifukwa cace zakucuruka zace adadzionera zatayika.

37. Pakuti mitu yonse iri yadazi, ndipo ndebvu ziri zosengedwa; pa manja onse pali pocekedwa-cekedwa, ndi pacuuno ciguduli.

38. Pamwamba pa macindwi a Moabu ndi m'miseu mwace muli kulira monse monse; pakuti ndaswa Moabu monga mbiya m'mene mulibe cikondwero, ati Yehova.

39. Yasweka bwanji! Akuwa bwanji Moabu! Wapotoloka bwanji ndi manyazi! Comweco Moabu adzakhala coseketsa ndi coopsera onse omzungulira iye.

40. Pakuti Yehova atero: Taonani, adzauluka ngati ciombankhanga, adzamtambasulira Moabu mapiko ace.

41. Keroti walandidwa, ndi malinga agwidwa, ndipo tsiku lomwelo mtima wa anthu amphamvu a Moabu adzakhala ngati mtima wa mkazi alinkudwala.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 48