Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 48:16-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Tsoka la Moabu layandikira kudza, nsautso yace ifulumiratu.

17. Inu nonse akumzungulira, mumcitire iye cisoni, inu nonse akudziwa dzina lace; muti, Cibonga colimba catyokatu, ndodo yokoma!

18. Iwe mwana wamkazi wokhala m'Diboni, utsike pa ulemerero wako, nukhale ndi ludzu; pakuti wakufunkha Moabu wakukwerera, iwe waononga malinga ako.

19. Iwe wokhala m'Aroeri, ima panjira, nusuzumire umfunse iye amene athawa, ndi mkazi amene apulumuka; nuti, Cacitidwa ciani?

20. Moabu wacitidwa manyazi, pakuti watyoka; kuwa nulire, nunene m'Arinoni, kuti Moabu wapasuka.

21. Ciweruzo cafika pa dziko lacidikha; pa Holoni, ndi pa Yaza, ndi pa Mefati;

22. ndi pa Diboni, ndi pa Nebo, ndi pa Beti-Dibilataimu;

23. ndi pa Kiriataimu, ndi pa Beti-Gamuli, ndi pa Beti-Meoni;

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 48