Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 48:14-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Muti bwanji, Tiri amphamvu, olimba mtima ankhondo?

15. Moabu wapasuka, akwera kulowa m'midzi yace, ndi anyamata ace osankhika atsikira kukaphedwa, ati Mfumu, dzina lace ndiye Yehova wa makamu.

16. Tsoka la Moabu layandikira kudza, nsautso yace ifulumiratu.

17. Inu nonse akumzungulira, mumcitire iye cisoni, inu nonse akudziwa dzina lace; muti, Cibonga colimba catyokatu, ndodo yokoma!

18. Iwe mwana wamkazi wokhala m'Diboni, utsike pa ulemerero wako, nukhale ndi ludzu; pakuti wakufunkha Moabu wakukwerera, iwe waononga malinga ako.

19. Iwe wokhala m'Aroeri, ima panjira, nusuzumire umfunse iye amene athawa, ndi mkazi amene apulumuka; nuti, Cacitidwa ciani?

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 48