Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 34:7-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. pamene nkhondo ya mfumu ya ku Babulo inamenyana ndi Yerualemu, ndi midzi yonse ya Yuda imene inatsala, ndi Lakisi ndi Azeka; pakuti midzi ya Yuda yamalinga yotsala ndi imeneyi.

8. Mau amene anadza kwa Yeremiya kucokera kwa Yehova, atapangana Zedekiya pangano ndi anthu onse amene anali pa Yerusalemu, kuti awalalikire iwo ufulu;

9. kuti yense ammasule kapolo wace wamwamuna, ndi wamkazi, pokhala iye Mhebri wamwamuna kapena wamkazi, kuti yense asayese Myuda mnzace kapolo wace;

10. ndipo akuru onse ndi anthu onse anamvera, amene anapangana mapangano, akuti yense ammasule kapolo wace wamwamuna, kapena wamkazi osawayesanso akapolo; iwo anamvera nawamasula;

11. koma pambuyo pace anabwerera, nabweza akapolo ace amuna ndi akazi, amene anawamasula, nawagonjetsanso akhale akapolo amuna ndi akazi;

12. cifukwa cace mau a Yehova anadza kwa Yeremiya kucokera kwa Yehova, kuti,

13. Yehova Mulungu wa Israyeli atero: Ndinapangana mapangano ndi makolo anu tsiku lija ndinawaturutsa m'dziko la Aigupto, kuturuka m'nyumba ya ukapolo, kuti,

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 34