Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 32:15-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Pakuti Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli atero: Nyumba ndi minda ndi minda yamphesa idzagulidwanso m'dziko muno.

16. Ndipo nditapereka kalata wogulirayo kwa Baruki mwana wa Neriya, ndinapemphera kwa Yehova, kuti,

17. Ha! Yehova Mulungu, taonani, Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi ndi mphamvu yanu yaikuru ndi mkono wanu wotambasuka; palibe cokulakani Inu;

18. a amene mucitira cifundo anthu zikwi; nimubwezera mphulupulu ya atate m'cifuwa ca ana ao a pambuyo pao, dzina lace ndi Mulungu wamkuru, wamphamvu, Yehova wa makamu;

19. wamkuru, m'upo, wamphamvu m'nchito; maso anu ali otsegukira njira zonse za ana a anthu; kuti mupatse yense monga mwa cipatso ca macitidwe ace;

20. amene munaika zizindikiro ndi zodabwitsa m'dziko la Aigupto, mpaka lero lomwe, m'Israyeli ndi mwa anthu ena; nimunadzitengera mbiri, monga lero lomwe;

21. ndipo munaturutsa anthu anu Israyeli m'dziko la Aigupto ndi zizindikiro, ndi zodabwitsa, ndi dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka, ndi mantha ambiri;

22. ndipo munawapatsa iwo dziko ili, limene munalumbirira makolo ao kuti mudzawapatsa, dziko moyenda mkaka ndi uci;

23. ndipo analowa, nakhalamo; koma sa namvera mau anu, sanayenda m'cilamulo canu; sanacita kanthu ka zonse zimene munawauza acite; cifukwa cace mwafikitsa pa iwo coipa conseci;

24. taonani mitumbira, yafika kumudzi kuugwira, ndipo mudzi uperekedwa m'dzanja la, Akasidi olimbana nao, cifukwa ca lupanga, ndi cifukwa ca njala, ndi cifukwa ca caola; ndipo cimene munacinena caoneka; ndipo, taonani, muciona.

25. Ndipo Inu Yehova Mulungu mwati kwa ine, Udzigulire munda ndi ndalama, nuitane mboni; koma mudzi waperekedwa m'manja a Akasidi.

26. Ndipo anadza mau a Yehova kwa Yeremiya, kuti,

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 32