Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 25:18-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Yerusalemu, ndi midzi ya Yuda, ndi mafumu ace omwe, ndi akuru ace, kuwayesa iwo bwinja, cizizwitso, cotsonyetsa, ndi citemberero; monga lero lino;

19. Farao mfumu ya ku Aigupto, ndi atumiki ace, ndi akuru ace, ndi anthu ace onse;

20. ndi anthu onse osanganizidwa, ndi mafumu onse a dziko la Uzi, ndi mafumu onse a dziko la Afilisti, ndi Asikeloni, ndi Gaza, ndi Ekroni, ndi otsala a Asdodi,

21. Edomu, ndi Moabu, ndi ana a Amoni,

22. ndi mafumu onse a Turo, ndi mafumu onse a Zidoni, ndi mafumu a cisumbu cimene ciri patsidya pa nyanja;

23. Dedani, ndi Tema, ndi Buzi, ndi onse amene ameta m'mbali mwa tsitsi;

24. ndi mafumu onse a Arabiya, ndi mafumu onse a anthu osanganizidwa okhala m'cipululu;

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 25