Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 20:13-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Muyimbire Yehova, mulemekeze Yehova; pakuti walanditsa moyo wa aumphawi m'dzanja la ocita zoipa.

14. Litembereredwe tsiku limene ndinabadwa; lisadalitsike tsiku limene amai wanga anandibala ine.

15. Atembereredwe munthu amene anatengera mau kwa atate wanga, kuti, Mwana wamwamuna anakubadwira iwe; ndi kumsekeretsatu iye.

16. Munthuyo akhale ngati midzi imene Yehova anapasula, osalekerera; amve mpfuu mamawa, ndi mkuwo pausana;

17. cifukwa sanandipha ine m'mimba; kuti mai wanga akhale manda anga, ndi mimba yace yaikuru nthawi zonse.

18. Cifukwa canji ndinaturuka m'mimba kuti ndione kutopa ndi kulira, kuti masiku anga athe ndi manyazi?

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 20