Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 2:33-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

33. Kodi sukonzadi njira yako kufunafuna cilakolako? cifukwa cace waphunzitsa akazi oipa njira zako.

34. Ndiponso m'nsaru zako wapezeka mwazi wa miyoyo ya aumphawi osacimwa; sunawapeza pakuboola, koma ponsepo.

35. Koma unati, Ndiri wosacimwa ndithu; mkwiyo wace wacoka pa ine. Taona, ndidzakuweruza iwe, cifukwa uti, Sindinacimwa.

36. Bwanji uyendayenda kwambiri ndi kusintha njira yako? udzacitanso manyazi ndi Aigupto monga unacita manyazi ndi Asuri.

37. Koma udzaturuka kwa iyenso, manja ako pamtu pako; pakuti Yehova wakana zokhulupirira zako, ndipo sudzapindula m'menemo.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 2