Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 2:28-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Koma iri kuti milungu yako imene wadzipangira? Iuke, ikupulumutse iwe m'nthawi ya kubvutidwa kwako; pakuti milungu yako ilingana ndi kucuruka kwa midzi yako, Yuda iwe.

29. Cifukwa canji mudzatsutsana ndi Ine nonse? mwandilakwira Ine, ati Yehova.

30. Ndapanda ana anu mwacabe; sanamvera kulanga; lupanga lanu ladya aneneri anu, monga mkango wakuononga.

31. Mbadwo inu, taonani mau a Yehova. Kodi ndakhala kwa Israyeli cipululu? Kapena dziko la mdima woti bii? Cifukwa ninji ati anthu anga, Tamasuka sitidzabweranso konse kwa Inu?

32. Kodi angathe namwali kuiwala zokometsera zace, kapena mkwatibwi zobvala zace? koma anthu anga andiiwala Ine masiku osawerengeka.

33. Kodi sukonzadi njira yako kufunafuna cilakolako? cifukwa cace waphunzitsa akazi oipa njira zako.

34. Ndiponso m'nsaru zako wapezeka mwazi wa miyoyo ya aumphawi osacimwa; sunawapeza pakuboola, koma ponsepo.

35. Koma unati, Ndiri wosacimwa ndithu; mkwiyo wace wacoka pa ine. Taona, ndidzakuweruza iwe, cifukwa uti, Sindinacimwa.

36. Bwanji uyendayenda kwambiri ndi kusintha njira yako? udzacitanso manyazi ndi Aigupto monga unacita manyazi ndi Asuri.

37. Koma udzaturuka kwa iyenso, manja ako pamtu pako; pakuti Yehova wakana zokhulupirira zako, ndipo sudzapindula m'menemo.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 2