Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Rute 4:15-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Nakhale uyu wakukubwezera moyo, ndi wodyetsa ukalamba wako; pakuti mpongozi wako amene akukonda, amene aposa ana amuna asanu ndi awiri kukuthandiza, anambala.

16. Ndipo Naomi anamtenga mwanayo, namuika pacifuwa pace, nakhala mlezi wace.

17. Ndi akazi anansi ace anamucha dzina, ndi kuti, Kwa Naomi kwambadwira mwana; namucha dzina lace Ohedi; ndiye atate wa Jese atate wa Davide.

18. Iyo ndiyo mibadwo ya Perezi; Perezi anabala Hezironi;

19. ndi Hezironi anabala Ramu, ndi Ramu anabala Aminadabu;

20. ndi Aminadabu anabala Nasoni, ndi Nasoni anabala Salimoni;

21. ndi Salimoni anabala Boazi, ndi Boazi anabala Obedi;

22. ndi Obedi anabala Jese, ndi Jese anabala Davide.

Werengani mutu wathunthu Rute 4