Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Rute 3:2-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Nanga Boazi wodziwana nafe, amene unakhala nao adzakazi ace? Taona, usiku uno apuntha barele popunthirapo.

3. Usambe tsono, nudzole, nubvale zobvala zako, nutsikire popunthirapo, koma usadziwike naye munthuyo, koma atatha kudya ndi kumwa ndiko.

4. Ndipo kudzali, akagona, upenye apo ati agone, numuke, nubvundukule ku mapazi ace, nugone, ndi iyeyo adzakufotokozera zoyenera kucita iwe.

5. Ndipo ananena naye, Zonse muzinena ndidzacita.

6. Pamenepo anatsikira popunthirapo, nacita zonse monga umo mpongozi wace adamuuza.

7. Ndipo atatha Boazi kudya ndi kumwa, nusekerera mtima wace, anakagona kuthungo kwa mulu wa tirigu; nadza iye kacetecete, nabvuodukula ku mapazi ace, nagona.

8. Ndipo kunali, pakati pa usiku munthuyo anadzidzimuka, natembenuka; ndipo taona pa mapazi ace pagona mkazi.

9. Nati iye, Ndiwe yani? Nayankha iye, Ndine Rute mdzakazi wanu; mupfunde mdzakazi wanu copfunda canu, pakuti inu ndinu wondiombolera colowa.

10. Nati iye, Yehova akudalitse, mwana wanga. Cokoma cako wacicita potsiriza pano, ciposa cakuyamba cija, popeza sunatsata anyamata, angakhale osauka angakhale acuma.

11. Ndipo tsopano, mwana wanga, usaope; ndidzakucitira zonse unenazi; pakuti onse a pa mudzi wa anthu a mtundu wanga adziwa kuti iwe ndiwe mkazi waulemu.

12. Tsopano ndipo, zoonadi, ine ndine wakukuombolera colowa, koma pali wakukuombolera woposa ine.

13. Gona usiku uno, ndipo kudzali m'mawa, akakuombolera, cabwino, akuombolere; koma ngati safuna kukuombolera, pali Yehova, ndidzakuombolera colowa ndine; gona mpaka m'mawa.

14. Nagona ku mapazi ace mpaka m'mawa; nalawira asanazindikirane anthu, Pakuti anati, Cisadziwike kuti mkaziyo anadza popunthirapo,

Werengani mutu wathunthu Rute 3