Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Rute 3:10-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Nati iye, Yehova akudalitse, mwana wanga. Cokoma cako wacicita potsiriza pano, ciposa cakuyamba cija, popeza sunatsata anyamata, angakhale osauka angakhale acuma.

11. Ndipo tsopano, mwana wanga, usaope; ndidzakucitira zonse unenazi; pakuti onse a pa mudzi wa anthu a mtundu wanga adziwa kuti iwe ndiwe mkazi waulemu.

12. Tsopano ndipo, zoonadi, ine ndine wakukuombolera colowa, koma pali wakukuombolera woposa ine.

13. Gona usiku uno, ndipo kudzali m'mawa, akakuombolera, cabwino, akuombolere; koma ngati safuna kukuombolera, pali Yehova, ndidzakuombolera colowa ndine; gona mpaka m'mawa.

14. Nagona ku mapazi ace mpaka m'mawa; nalawira asanazindikirane anthu, Pakuti anati, Cisadziwike kuti mkaziyo anadza popunthirapo,

Werengani mutu wathunthu Rute 3