18. Ndipo pakuona kuti analimbika kumuka naye, analeka kulankhula naye.
19. Namuka iwo awiriwo mpaka anafika ku Betelehemu. Ndipo kunali pakufika iwo ku Betelehemu, mudzi wonse unapokosera za iwo; nati, Kodi uyu ndi Naomi?
20. Koma ananena nao, Musandicha Naomi, mundiehe Mara; pakuti Wamphamvuyonse anandicitira zowawa ndithu.
21. Ndinacoka pane wolemera, nandibwezanso kwathu Yehova wopanda kanthu; mundicheranji Naomi, popeza Yehova wandicitira umboni wakunditsutsa, ndi Wamphamvuyonse wandicitira cowawa?