Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Rute 1:18-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo pakuona kuti analimbika kumuka naye, analeka kulankhula naye.

19. Namuka iwo awiriwo mpaka anafika ku Betelehemu. Ndipo kunali pakufika iwo ku Betelehemu, mudzi wonse unapokosera za iwo; nati, Kodi uyu ndi Naomi?

20. Koma ananena nao, Musandicha Naomi, mundiehe Mara; pakuti Wamphamvuyonse anandicitira zowawa ndithu.

21. Ndinacoka pane wolemera, nandibwezanso kwathu Yehova wopanda kanthu; mundicheranji Naomi, popeza Yehova wandicitira umboni wakunditsutsa, ndi Wamphamvuyonse wandicitira cowawa?

Werengani mutu wathunthu Rute 1