Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 5:17-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Gileadi anakhala tsidya lija la Yordano;Ndi Dani, akhaliranji mzombo?Aseri anakhala pansi m'mphepete mwa nyanja,Nakhalitsa pa nyondo yace ya nyanja.

18. Zebuloni ndiwo anthu anataya moyo wao mpaka imfa,Nafitali yemwe poponyana pamisanje.

19. Anadza mafumu, nathira nkhondoPamen'epo anathira nkhondo mafumu a Kanani.M'Taanaki, ku madzi a Megido;Osatengako phindu la ndarama.

20. Nyenyezi zinathira nkhondo yocokera kumwamba,M'mipita mwao zinathirana ndi Sisera.

21. Mtsinje wa Kisoni unawakokolola,Mtsinje uja wakale, mtsinje wa Kisoni.Yenda mwamphamvu, moyo wangawe.

22. Pamenepo ziboda za akavalo zinaguguda,Ndi kutumphatumpha, kurumphatumpha kwa anthu ace eni mphamvu,

23. Mutemberere Merozi, ati mthenga wa Yehova,Mutemberere citemberere nzika zace;Pakuti sanadzathandiza Yehova,Kumthandiza Yehova pa acamuna.

24. Wodalitsika, woposa akazi, akhale YaeliMkazi wa Heberi Mkeni.Akhale wodalitsika woposa akazi a m'hema.

25. Mwamunayo anapempha madzi, anampatsa mkaka,Anamtengera mafuta a mkaka m'cotengera ca mfulu.

26. Dzanja lace analitambasulira kuciciri,Ndi dzanja lace lamanja ku nyundo ya anchito,Nakhomera Sisera, nakantha mutu wace,Inde, anaphwanya napyoza m'litsipa mwace.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 5